Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Makolo asiya mwana pa golosale

Apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre akusunga mwana amene akuti makolo ake anamusiya pa golosale ina kwa Manje.

Ofalitsankhani pa Polisi ya Limbe, a Aubrey Singanyama, ati mwanayu dzina lake ndi Beatrice ndipo ndi wa mkazi komanso akuganizira kuti atha kukhala ndi zaka zapakati pa ziwiri kapena zitatu.

A Singanyama ati anthu amene akumudziwa mwanayu apite ku polisiyi mwamsanga kapena akauze a polisi amene ali nawo pafupi.

Related posts

Lizulu ikhala tauni yaying’ono — Dr Chakwera

Romeo Umali

‘Kalembetseni chiphaso cha unzika kuti mudzavote’

Romeo Umali

‘Osakakamira wachikondi wankhanza’

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.