Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Majaji agwidwa ndi chisoni ndi imfa ya Kasambara

Majaji m’dziko muno ati ali ndi chisoni kaamba ka imfa ya a Raphael Kasambara omwe anali katswiri wa za malamulo komanso yemwe anathandiza kwambiri polimbikitsa ntchito zamalamulo m’dziko muno.

Justice Zione Ntaba, anena izi pamwambo otsanzikana ndi a Kasambara omwe ukuchitikira kunyumba kwa malemuwa ku Nyambadwe mu mzinda wa Blantyre.

Posachedwapa, maliro apita nawo ku CI komwe kukachitikire mapemphero asananyamule thupi la Malemuwa pa ndege kupita kumudzi kwawo m’boma la Nkhata Bay komwe akaliyike m’manda lolemba.

A Michael Usi, nduna yazosamalira chilengedwe, ndiwo akuimira boma pa mwambowu.

 

Related posts

President Chakwera pledges to continue protecting workers’ rights

MBC Online

Silver dominates NBM Premiership

MBC Online

Jenda Police seize 27 motorcycles for traffic violation

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.