Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Majaji agwidwa ndi chisoni ndi imfa ya Kasambara

Majaji m’dziko muno ati ali ndi chisoni kaamba ka imfa ya a Raphael Kasambara omwe anali katswiri wa za malamulo komanso yemwe anathandiza kwambiri polimbikitsa ntchito zamalamulo m’dziko muno.

Justice Zione Ntaba, anena izi pamwambo otsanzikana ndi a Kasambara omwe ukuchitikira kunyumba kwa malemuwa ku Nyambadwe mu mzinda wa Blantyre.

Posachedwapa, maliro apita nawo ku CI komwe kukachitikire mapemphero asananyamule thupi la Malemuwa pa ndege kupita kumudzi kwawo m’boma la Nkhata Bay komwe akaliyike m’manda lolemba.

A Michael Usi, nduna yazosamalira chilengedwe, ndiwo akuimira boma pa mwambowu.

 

Related posts

TWO MORE TO TESTIFY IN CHISALE CASE

MBC Online

Homeland Ministry talks tough on human trafficking

Romeo Umali

Ascent crowned Goshen- FAM Women’s Championship

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.