Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Loya amangidwa pomuganizira kuti ali ndi galimoto yobedwa

Apolisi anjata a Stanley Chirwa, amene ndi oyimira anthu pamilandu (lawyer), powaganizira kuti ali ndi galimoto la mtundu wa Ford Ranger limene lidabedwa ndi zigawenga za mfuti m’dziko la South Africa, m’chaka cha 2018.

Mneneri wa apolisi m’dziko muno, a Peter Kalaya, ati galimotoyi a Chirwa anapita nayo kokayilembetsa pa 8 April 2024, koma iwo anapeza kuti galimotoyi ikufanana ndi yomwe idabedwa ndi mbala zaku South Africa, malinga ndi zopeza za apolisi a m’dzikolo.

A Kalaya ati bambowa akukanika kufotokoza komwe iwo adagula galimotoyi koma ati apolisi afufuza kuti apeze choonadi.

A Chirwa akuyembekezeka kuwatsekulira milandu ingapo, kuphatikizapo kulandira kapena kubweretsa katundu wakunja popanda chilungamo, komanso kupezeka ndi katundu amene akumuganizira kuti ndi obedwa.

 

Related posts

2 WIN BIG WITH BETIKA

Rabson Kondowe

Players in the water sector discuss non-revenue water

Romeo Umali

Prophet Bushiri donates K30m to Area 43 Police Unit construction

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.