Malawi Broadcasting Corporation
Africa Development Local Local News Nkhani

Achinyamata asamalire okalamba — Mayi Mbambande

“Achinyamata asinthe maganizo awo poona anthu okalamba ngati mfiti,” izi ndi zimene anayankhula Deborah Mbale, mwini wake wa Mayi Mbambande, malo amene amasamalirako anthu okalamba.

Iye wanena izi pamene amalandira thandizo landalama zokwana K1 million kuchokera ku kampani ya Chisurija Transportation Services (CTS).

Jaquelin Bokosi, amene ndi mwini wa kampaniyi CTS, wati anaganiza zopereka thandizoli kaamba kakuti malo a Mayi Mbambande akugwira ntchito yobweretsa chimwemwe kwa anthu achikulire.

A Nasitima Chikadwala, omwe ndi m’modzi mwa anthu okalamba zedi omwe akukhala pa malopa, anati malowa, omwe ali m’mudzi wa Dzama kwa Mfumu yaikulu Chitukula ku Lilongwe, anawachotsa chitonzo chifukwa iwo akusamalidwa.

Padakali pano, malowa akuyang’anira anthu okalamba okwana 85.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malaulo: Anjatidwa atagwililira mwana omupeza pofuna kukhwima

Charles Pensulo

Scientists discover 127 new species native to Malawi, Mozambique

MBC Online

There was overuse of antibiotics during COVID — WHO report

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.