Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Kuchedwa kwa nsewu wa Ilomba kwadandaulitsa boma

Boma lati ndilokhumudwa ndi momwe ntchito yomanga msewu ochokera ku Chitipa kupita ku Ilomba ikuchedwera kufika kumapeto.

Nduna yoona za mtengatenga, a Jacob Hara, ndiwo anena izi ku Chitipa atayendera ntchito yomanga msewuwu.

Iwo ati boma linapereka ntchitoyi kwa kampani za m’dziko mom’muno koma ati ndiokhumudwa ndimomwe kampanizi zikuchedwetsera ntchitoyi.

“Momwe taonera ntchitoyi, taganiza zobweretsa makampani ena kuti athandize makampani omwe ali kunowa kuti ntchitoyi ithe msanga,” anatero a Hara.

Mfumu Mwawulambya ya m’bomali yati ili ndichikhulupiliro kuti tsopano ntchitoyi iyamba kuyenda bwino, potengera ndi zomwe ndunayi yanena.

Msewu wa Chitipa Ilomba ndiotalika makilomita 30.

Wolemba: Henry Haukeya

Related posts

Asilikali agwira nzika 276 zozembetsedwa zaku Ethiopia

Romeo Umali

Mfumu Ngokwe yayamika magulu akufuna kwabwino

Alinafe Mlamba

Baba Malondera lauds Chakwera’s administration

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.