Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

FAM ikusaka ma passport a Flames

Mkulu ofalitsankhani komanso kuyendetsa mipikisano ku bungwe la FAM, a Gomezgani Zakazaka, ati ntchito yofufuza ma passport a osewera atimu ya Flames omwe asowa m’dziko la Mali ikupitilirabe.

Malinga ndi malipoti, m’modzi mwa akuluakulu a timuyi anaiwala ma passport amenewa mu taxi yomwe anakwera.

Malawi ili m’dziko la Mali pomwe usiku uno ikuyembekezeka kuti isewele ndi timu ya Burkina Faso mu masewero a mu ndime yodzigulira malo ku mpikisano wa AFCON.

Kanema za MBC komanso wailesi ya Radio 2 fm zilengezera masewero wa omwe ayambe 9 koloko usiku uno.

 

Olemba: Amin Mussa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MITC urge producers to increase value-added exports

Aisha Amidu

STANDARD BANK LINKS UNAYO TO AUTOMATED TELLER MACHINES

McDonald Chiwayula

A Chisale akuyankha mulandu

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.