Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

FAM ikusaka ma passport a Flames

Mkulu ofalitsankhani komanso kuyendetsa mipikisano ku bungwe la FAM, a Gomezgani Zakazaka, ati ntchito yofufuza ma passport a osewera atimu ya Flames omwe asowa m’dziko la Mali ikupitilirabe.

Malinga ndi malipoti, m’modzi mwa akuluakulu a timuyi anaiwala ma passport amenewa mu taxi yomwe anakwera.

Malawi ili m’dziko la Mali pomwe usiku uno ikuyembekezeka kuti isewele ndi timu ya Burkina Faso mu masewero a mu ndime yodzigulira malo ku mpikisano wa AFCON.

Kanema za MBC komanso wailesi ya Radio 2 fm zilengezera masewero wa omwe ayambe 9 koloko usiku uno.

 

Olemba: Amin Mussa

Related posts

Govt urges farmers to adopt new farming technologies

Romeo Umali

Chakwera outlines measures to address soil degradation

Rabson Kondowe

Mangochi Police drill Kabaza operators on road safety

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.