Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

Deposit Insurance Corporation ayikhazikitsa sabata lamawa

Anthu omwe amasungitsa ndalama zawo mu banki zosiyasiyana m’dziko muno akhala ndi chitsimikizo chochuluka cha chitetezo pa nthawi yomwe bank zingalephere kupitiriza ntchito.

Izi zili chomwecho chifukwa boma lidakhazikitsa nthambi yotchedwa Deposit Insurance Corporation (DIC) imene aitsekulire sabata lamawa.

Nthambiyi anayikhazikitsa kudzera mu lamulo kuti idzipereka insurance kwa kampani zosunga ndalama, ndicholinga choteteza anthu osungitsa ndalamazo.

Poyankhula pa maphunziro a olembankhani zamalonda ndi chuma, mkulu wa nthambi ya DIC, a Chitani Chigumula, ati malinga ndi lamulo la DIA, banki zonse zomwe zili ndi chiphaso zikuyenera kukhala pa sikimu yomwe zidzidulidwa ndalama yolingana ndi kukula kwa chiwerengero cha ndalama zomwe akusunga.

 

Related posts

Sean Morgan to release his first song for 2024

Romeo Umali

Ekhaya claim second spot

Romeo Umali

PRISAM demands arrests over school vandalism

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.