Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

Deposit Insurance Corporation ayikhazikitsa sabata lamawa

Anthu omwe amasungitsa ndalama zawo mu banki zosiyasiyana m’dziko muno akhala ndi chitsimikizo chochuluka cha chitetezo pa nthawi yomwe bank zingalephere kupitiriza ntchito.

Izi zili chomwecho chifukwa boma lidakhazikitsa nthambi yotchedwa Deposit Insurance Corporation (DIC) imene aitsekulire sabata lamawa.

Nthambiyi anayikhazikitsa kudzera mu lamulo kuti idzipereka insurance kwa kampani zosunga ndalama, ndicholinga choteteza anthu osungitsa ndalamazo.

Poyankhula pa maphunziro a olembankhani zamalonda ndi chuma, mkulu wa nthambi ya DIC, a Chitani Chigumula, ati malinga ndi lamulo la DIA, banki zonse zomwe zili ndi chiphaso zikuyenera kukhala pa sikimu yomwe zidzidulidwa ndalama yolingana ndi kukula kwa chiwerengero cha ndalama zomwe akusunga.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chakwera seeks global support for Malawi’s digital exploits

Mayeso Chikhadzula

Muslims urged to advocate for peace and stability in Malawi

Sothini Ndazi

Chisemphere FC wins Mike Bango trophy

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.