Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

Deposit Insurance Corporation ayikhazikitsa sabata lamawa

Anthu omwe amasungitsa ndalama zawo mu banki zosiyasiyana m’dziko muno akhala ndi chitsimikizo chochuluka cha chitetezo pa nthawi yomwe bank zingalephere kupitiriza ntchito.

Izi zili chomwecho chifukwa boma lidakhazikitsa nthambi yotchedwa Deposit Insurance Corporation (DIC) imene aitsekulire sabata lamawa.

Nthambiyi anayikhazikitsa kudzera mu lamulo kuti idzipereka insurance kwa kampani zosunga ndalama, ndicholinga choteteza anthu osungitsa ndalamazo.

Poyankhula pa maphunziro a olembankhani zamalonda ndi chuma, mkulu wa nthambi ya DIC, a Chitani Chigumula, ati malinga ndi lamulo la DIA, banki zonse zomwe zili ndi chiphaso zikuyenera kukhala pa sikimu yomwe zidzidulidwa ndalama yolingana ndi kukula kwa chiwerengero cha ndalama zomwe akusunga.

 

Related posts

Gender Ministry highlights importance of reporting on social protection programmes

Rabson Kondowe

Govt, FAO sign K90.6 billion pact to enhance Ecosystem-Based Adaptation Project

McDonald Chiwayula

Local insurance industry catches the digital penetration euphoria

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.