Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

Deposit Insurance Corporation ayikhazikitsa sabata lamawa

Anthu omwe amasungitsa ndalama zawo mu banki zosiyasiyana m’dziko muno akhala ndi chitsimikizo chochuluka cha chitetezo pa nthawi yomwe bank zingalephere kupitiriza ntchito.

Izi zili chomwecho chifukwa boma lidakhazikitsa nthambi yotchedwa Deposit Insurance Corporation (DIC) imene aitsekulire sabata lamawa.

Nthambiyi anayikhazikitsa kudzera mu lamulo kuti idzipereka insurance kwa kampani zosunga ndalama, ndicholinga choteteza anthu osungitsa ndalamazo.

Poyankhula pa maphunziro a olembankhani zamalonda ndi chuma, mkulu wa nthambi ya DIC, a Chitani Chigumula, ati malinga ndi lamulo la DIA, banki zonse zomwe zili ndi chiphaso zikuyenera kukhala pa sikimu yomwe zidzidulidwa ndalama yolingana ndi kukula kwa chiwerengero cha ndalama zomwe akusunga.

 

Related posts

KAWINGA FC CLINCH CHIPIKU LEAGUE TITLE, EARN SUPER LEAGUE PROMOTION 

Romeo Umali

NYALONJE URGES WOMEN TO REPORT SEXUAL ABUSE IN WORKPLACES

Romeo Umali

GUTERRES OPENS UNGA WITH A CALL FOR PEACE

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.