Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Sing’anga akakhala kundende pamlandu ogwililira

Bwalo lamilandu ku Zomba lalamula mwamuna wazaka 55, Bamus Wilesi, kukakhala kundende zaka 16 atapezeka wolakwa pamlandu ogwililira mtsikana wazaka 14 yemwe anamupatsa K2,000 kuti asawulure.

Ofalitsankhani wapolisi ku Zomba, Patricia Sipiliano, wati mtsikanayo amakonda kudutsa pakhomo pa Wilesi, yemwenso ndi sing’anga, popita kukatunga madzi komanso ku chigayo.

Tsiku lina, sing’angayo ananyengelera mwanayo ndikugona naye kenako anamupatsa ndalamayo ngati chitseka pakamwa.

Koma atafika kunyumba kwawo, mtsikanayo anatulutsa ndalamayo kunyaditsa amzake makolo ake akuwona.

Atamufunsa, iye anaulura za nkhaniyo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mozambique dangles business opportunities in Tete

Justin Mkweu

Nkhatabay people benefit from SSRLP

MBC Online

Tiyeni tipitirize kumvera mtsogoleri komanso kukonda chipani chathu — Msukwa

Olive Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.