Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Sing’anga akakhala kundende pamlandu ogwililira

Bwalo lamilandu ku Zomba lalamula mwamuna wazaka 55, Bamus Wilesi, kukakhala kundende zaka 16 atapezeka wolakwa pamlandu ogwililira mtsikana wazaka 14 yemwe anamupatsa K2,000 kuti asawulure.

Ofalitsankhani wapolisi ku Zomba, Patricia Sipiliano, wati mtsikanayo amakonda kudutsa pakhomo pa Wilesi, yemwenso ndi sing’anga, popita kukatunga madzi komanso ku chigayo.

Tsiku lina, sing’angayo ananyengelera mwanayo ndikugona naye kenako anamupatsa ndalamayo ngati chitseka pakamwa.

Koma atafika kunyumba kwawo, mtsikanayo anatulutsa ndalamayo kunyaditsa amzake makolo ake akuwona.

Atamufunsa, iye anaulura za nkhaniyo.

Related posts

Portland can generate forex — Tembo

Romeo Umali

Thyolo ramps up efforts to bolster Covid-19 Vaccine uptake

Romeo Umali

Israeli heart surgeries change lives of Malawians

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.