Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dekhani AMalawi zikutheka — Chakwera

Prezidenti wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, watsimikizira anthu a m’boma la Dowa kuti vuto la madzi likhala mbiri ya makedzana.

Poyankhula kwa khwimbi la anthu limene linasonkhana pa Madisi Trading Centre, Dr Chakwera wati kubwera kwa chitukuko cha madzi Cha Kholongo Multipurpose Dam zithandizira kwambiri kusintha miyoyo ya anthu a m’boma la Dowa ndi madela wozungulira.

Pa chifukwachi, mtsogoleri wa dziko linoyu wapempha aMalawi kuti adekhe pomwe akukhazikitsa zitukuko zosiyanasiyana mokomera aMalawi onse.

Chitukuko cha madzi cha Kholongo Multipurpose Dam chikuyembekeza kutha chaka cha mawa.

Related posts

Mwambo wa Kulamba ulipo chaka chino

McDonald Chiwayula

Chiwalo’s appointment draws mixed reaction

MBC Online

Achinyamata asamalire okalamba — Mayi Mbambande

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.