Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Chilungamo pa malonda ndichofunika’

Bungwe la Malawi Bureau Standards (MBS) lati kugwira ntchito limodzi ndi nthambi zina zaboma nkofunika pa ntchito zolimbikitsa chilungamo pa malonda, mwazina.

Mkulu wa bungweli, a Ben Thole, anena izi pa mkumano omwe MBS linakonzera apolisi komanso owona za malonda m’makhonsolo am’chigawo chakumpoto.

A Thole ati ndi cholinga cha MBS kuonetsetsa kuti pali chilungamo pa malonda komanso kuti amalonda akugwiritsa ntchito milingo yoyenelera pogulitsa malonda awo.

“Tikufuna amalonda adzigulitsa katundu wa mulingo komanso muyeso oyenelera, zonsezi nzothandiza kuti anthu akugula katundu oyenelera komanso otetezedwa,” walongosola Thole.

Mikumano yotere yachitika kale m’zigawo zakummwera ndi pakati.

Olemba: George Mkandawire

Related posts

Malawi ipindula ndi ntchito yotukula luso lazaumoyo

Romeo Umali

ACHINYAMATA A CHIPANI CHA MCP ATHANDIZA PACHIPATALA CHA AREA 25 KU LILONGWE

MBC Online

FAM ikufuna abale ambiri kumpira wa miyendo

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.