Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikho cha Mayor’s chafika kumapeto ku Mzuzu

Bwalo lazamasewero la Katoto lero latangwanika chifukwa kukuchitika ndime yotsiriza ya chikho cha Mayor’s cha masewero a Mpira wamiyendo komanso wamanja.

Mwambowo wayamba ndi ulendo wa ndawala kuchoka kuma office a Mzuzu City Council kuyenda mu Highway kukafika pabwalo lazamasewero la Katoto.

Ena mwa amene anali nawo pa ulendowu ndi Mayor wa Mzinda wa Mzuzu a Kondwani Nyasulu, mkulu oyendetsa ntchito za mu mzindawo a Gomezgani Nyasulu, ma Khansala, ndi adindo ena osiyanasiyana kuphatikizapo akukuakulu a bank ya FDH amene akuthandiza chikhochi ndi ndalama zokwana K17 million.

Matimu a primary school a Zolozolo akumana ndi Chibavi mu masewero a mpira wa manja, pamene matimu a Mzuzu CCAP akumana ndi Katoto Primary School mu ndime yotsiliza ya Mpira wamiyendo wa anyamata.

 

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

NATIONAL PRODUCT MAGAZINE GETS REGIONAL RECOGNITION

Mayeso Chikhadzula

CHAKWERA TO LAUNCH  NEW NATIONAL YOUTH POLICY

MBC Online

Mayi amangidwa atamenya mwana wake mwankhanza ndikumutsira chitedze

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.