Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikho cha Mayor’s chafika kumapeto ku Mzuzu

Bwalo lazamasewero la Katoto lero latangwanika chifukwa kukuchitika ndime yotsiriza ya chikho cha Mayor’s cha masewero a Mpira wamiyendo komanso wamanja.

Mwambowo wayamba ndi ulendo wa ndawala kuchoka kuma office a Mzuzu City Council kuyenda mu Highway kukafika pabwalo lazamasewero la Katoto.

Ena mwa amene anali nawo pa ulendowu ndi Mayor wa Mzinda wa Mzuzu a Kondwani Nyasulu, mkulu oyendetsa ntchito za mu mzindawo a Gomezgani Nyasulu, ma Khansala, ndi adindo ena osiyanasiyana kuphatikizapo akukuakulu a bank ya FDH amene akuthandiza chikhochi ndi ndalama zokwana K17 million.

Matimu a primary school a Zolozolo akumana ndi Chibavi mu masewero a mpira wa manja, pamene matimu a Mzuzu CCAP akumana ndi Katoto Primary School mu ndime yotsiliza ya Mpira wamiyendo wa anyamata.

 

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

APEMPHA AKUFUNA KWABWINO KUTHANDIZA CHIPATALA CHA NKHOTAKOTA

Romeo Umali

MINISTRY OF HEALTH AGAINST SENSATIONAL REPORTING

MBC Online

Launch 16 Days of Activism against GBV underway

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.