Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Chakhala chaka chopambana – M’bawa

Nthambi yaza ndende mchigawo chakummwera yati chaka cha 2024 chakhala chopambana mukagwiridwe kawo ka ntchito.

Izi ndi malinga ndi mkulu wa nthambiyi mchigawochi, a Zacheus M’bawa.

Poyankhula pa mwambo osangalalira mmene nthambiyi yagwilira ntchito, a M’bawa ati m’chakachi, mwazina, achepetsa chiwerengero cha akaidi othawa mndende, alimbikitsa ulimi wambewu ndi ziweto komanso alimbikitsa ntchito zoonetsetsa kuti anthu amene anali ku ndende akulandiridwa bwino mmadera awo akamaliza kugwira zilango zawo.

Pamenepa, iwo ati m’chaka chikudzachi cha 2025 alimbikitsa ntchito za ulimi mndende za Mwanza, Bvumbwe ndi Mulanje kuti nthambiyi ipitilire kukhala yodzidalira kugawo la chuma ndi chakudya.

Pamwambowu, umene unachitikira ku Mulanje, panafika ogwira ntchito zandende ochokera ku Chikwawa, Thyolo, Bvumbwe ndi Nsanje.

Gulu loimba la Prison Strings Band ndilomwe linasangalatsa anthuwa usiku onse.

 

Olemba: Geoffrey Chinawa

Related posts

CHURCH DONATES RELIEF FOOD IN ZOMBA

Romeo Umali

Journalists drilled on New Pension Law

Romeo Umali

Gwengwe hails AVC as an economic driver

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.