Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bus ya Bullets inakalibe mmanja mwa khothi

Bus ya FCB Nyasa Big Bullets sinabwerere kuma ofesi atimuyi, dzulo italandidwa ndi ma Sherrif.

Bus-yi inalandidwa kaamba koti timuyi inali ndi ngongole ya ndalama zokwana K25 million ndi mphunzitsi wawo wakale Franco Ndawa.

Malingana ndi modzi mwa akuluakulu a Bullets, a Albert Chigoga, timuyi yalipira ndalamayi kuphatikizapo K4 million ndipo akudikira ndondomeko zokhudza malamulo kuti bus-yi ibwerere zomwe akuyendetsa ndi owayimira pamilandu.

Chigoga watsutsaso kuti timuyi ili ndi malingaliro ochotsa osewera ena pazifukwa kuti akupangila dala kuti timuyi isamachite bwino.

Lachiwiri, osewera a Bullets anakana kuchita zokonzekera za timuyi.

 

By Praise Majawa

Related posts

Nurses body unveils Malawi’s first Journal of Nursing

Romeo Umali

MCP WELCOMES CHANGA K, OTHERS IN NKHATABAY

MBC Online

Tourism Ministry for improved wildlife management

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.