Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bus ya Bullets inakalibe mmanja mwa khothi

Bus ya FCB Nyasa Big Bullets sinabwerere kuma ofesi atimuyi, dzulo italandidwa ndi ma Sherrif.

Bus-yi inalandidwa kaamba koti timuyi inali ndi ngongole ya ndalama zokwana K25 million ndi mphunzitsi wawo wakale Franco Ndawa.

Malingana ndi modzi mwa akuluakulu a Bullets, a Albert Chigoga, timuyi yalipira ndalamayi kuphatikizapo K4 million ndipo akudikira ndondomeko zokhudza malamulo kuti bus-yi ibwerere zomwe akuyendetsa ndi owayimira pamilandu.

Chigoga watsutsaso kuti timuyi ili ndi malingaliro ochotsa osewera ena pazifukwa kuti akupangila dala kuti timuyi isamachite bwino.

Lachiwiri, osewera a Bullets anakana kuchita zokonzekera za timuyi.

 

By Praise Majawa

Related posts

Trucker dies in his sleep

Romeo Umali

Hilal Africa treats over 3000 muslims in Salima to a feast

Romeo Umali

International Blantyre Cancer Centre Inaugurated

Secret Segula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.