Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

Boma lalimbikitsa ulimi

Unduna wa za ulimi wakhazikitsa ntchito yopereka feteleza wangongole kwa alimi a m’ma boma a Chikwawa ndi Nsanje.

Ntchitoyi ili pansi pa bungwe la National Economic Empowerment Fund (NEEF).

Nduna ya za ulimi, a Sam Kawale, ayankhula izi pamwambo okhazikitsa ntchitoyi mdera la mfumu yayikulu Maseya m’boma la Chikwawa.

A Kawale ati ndondomeko yopereka feteleza pangongoleyi ndi chiyambi chosintha ntchito za ulimi kuti zikule mpakana alimi atafika pomagwiritsa ntchito zinthu monga ma thalakitale polima.

Mkulu wa NEEF, a Humphrey Mdyetseni, anati pofika lero apereka feteleza kwa alimi pafupifupi 36,000.

Polankhula ku Nsanje, mfumu yaikulu Mlolo yalimbikitsa alimi opindula kuti agwiritse bwino ntchito fetelezayu komanso akumbukire kubwenza ngongole.

Ntchito yogawa feteleza m’ma bomawa inayamba miyezi ingapo yapitayo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Government commits to youth development through digital initiatives

Davie Umar

SHUGA ADZIPEZEKA OKWANIRA – ILLOVO

Justin Mkweu

Land dispute case adjourned to September

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.