Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lagawa chimanga ku Zomba

Boma lakhazikitsa ntchito yogawa chimanga kwa mabanja pafupifupi 8000 amene njala inawakhudza munzinda wa Zomba.

Mwambo okhazikitsa ntchitoyi unachitika Lachitatu ku Matawale kwa mfumu yayikulu Mwambo munzindawu.

Mkulu wa khonsolo ya Zomba, Archangel Bakolo, wati thandizolo labwera mu nthawi yake kaamba kakuti anthu 17 mwa anthu 100 aliwonse ndi amene njala idawakhudza.

Kudzera ku DoDMA, boma likhala likupereka chimangacho kwa miyezi isanu kuchokera mwezi uno.

Banja lililonse likulandira thumba lolemera makilogalamu 50.

Related posts

4 years in prison for theft of cattle

Romeo Umali

NEEF yakhazikitsa ngongole ya ulimi wa mthilira

Mayeso Chikhadzula

NFRA board ponders maize purchase commencement

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.