Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lagawa chimanga ku Zomba

Boma lakhazikitsa ntchito yogawa chimanga kwa mabanja pafupifupi 8000 amene njala inawakhudza munzinda wa Zomba.

Mwambo okhazikitsa ntchitoyi unachitika Lachitatu ku Matawale kwa mfumu yayikulu Mwambo munzindawu.

Mkulu wa khonsolo ya Zomba, Archangel Bakolo, wati thandizolo labwera mu nthawi yake kaamba kakuti anthu 17 mwa anthu 100 aliwonse ndi amene njala idawakhudza.

Kudzera ku DoDMA, boma likhala likupereka chimangacho kwa miyezi isanu kuchokera mwezi uno.

Banja lililonse likulandira thumba lolemera makilogalamu 50.

Related posts

Silver Strikers suffer first defeat

Romeo Umali

MEHA for pandemic mitigation strategies

Romeo Umali

First Lady urges action on education, youth poverty

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.