Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lagawa chimanga ku Zomba

Boma lakhazikitsa ntchito yogawa chimanga kwa mabanja pafupifupi 8000 amene njala inawakhudza munzinda wa Zomba.

Mwambo okhazikitsa ntchitoyi unachitika Lachitatu ku Matawale kwa mfumu yayikulu Mwambo munzindawu.

Mkulu wa khonsolo ya Zomba, Archangel Bakolo, wati thandizolo labwera mu nthawi yake kaamba kakuti anthu 17 mwa anthu 100 aliwonse ndi amene njala idawakhudza.

Kudzera ku DoDMA, boma likhala likupereka chimangacho kwa miyezi isanu kuchokera mwezi uno.

Banja lililonse likulandira thumba lolemera makilogalamu 50.

Related posts

Malawi Prison Service faces recurrent challenges in 2024

Yamikani Simtowe

Accurate reporting is key — Kunkuyu

Romeo Umali

‘Ntchito ya maphunziro ndi umoyo wabwino m’sukulu ikonzedwenso’

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.