Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bangwe yapha Bullets

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonja ndi timu ya Bangwe All Stars 1-0 pa bwalo la masewero la Kamuzu kudzera mu chigoli cha James Msowoya.

Aka ndi kugonja kachitatu kwa Bullets mu 2024 TNM Super League imene ili pa nambala khumi pa mdandanda wa matimu amu ligiyi.

Kupambanaku, zikutanthauza kuti Bangwe tsopano ili ma nambala 15 pa mdandanda wa matimuwa ndi ma point okwananso 15.

Awatu ndi masewero oyamba kuti timuyi igonjetse amene akusungira chikhochi komanso koyamba kuti achinye pagolo pawo pamasewero asanu amene asewera limodzi.

Komanso, awa anali masewero achiwiri a Trevor Kajawa chilhalireni ngati mphunzitsi wa tsopano wa Bangwe.

 

Olemba: Praise Majawa

Related posts

ROYAL FAMILY GATHERS AT BALMORAL AMID CONCERNS FOR QUEEN’S HEALTH

MBC Online

CMC to hold special camp meeting next year

McDonald Chiwayula

Chakwera ndi chiyembekezo cha dziko lino – Chimwendo Banda

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.