Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Azaumoyo akufufuza za imfa ya achinyamata aku Manase

Mu chinthuzi: Gift Kawalazira – Dotolo otsogolera ntchito zaumoyo ku Blantyre

Akuluakulu oona za umoyo munzinda wa Blantyre ati akufufuza za achinyamata ena amene malipoti akusonyeza kuti amwalira atamwa mowa wina  mdera la Manase mumzindawu.

Kalata imene yasayinidwa ndi dotolo otsogolera ntchito za zaumoyo ku Blantyre, a Gift Kawalazira, ikusonyeza kuti kafukufuku wa azachipatala wapeza kuti achinyamata asanu ndiwo amwalira pamene ena awiri akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha Queen Elizabeth atamwa mowa umene akuuganizira kuti wadwalitsa anyamata awiriwo ndinso kupha asanu enawo.

Anthu ena ati achinyamata ambiri akumakonda kumwa mowawo mma shabeen, umene ndiwaukali ndipo ena akuutchula kuti ‘mbuye tengeni’.

 

Related posts

All set for MIAC symposium

Rabson Kondowe

Masukambiya Health Post construction excites residents

Secret Segula

Akubanja la Chilima ayamika boma ndi a Malawi

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.