Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Anthu 87 a zipani zosiyanasiyana alowa MCP ku Mangochi

Anthu osachepera 80 ochokera zipani za DPP, UDF ndi zina alowa chipani cholamula cha Malawi Congres (MCP) ku Mangochi.

Powalandira anthuwa, yemwe ali wachiwiri kwa mkulu wa chipanichi ku chigawo cha kummawa, a Hassan Chikuta, anati anthu akulowa chipani cha MCP chifukwa cha mfundo zake zokhwima komanso anthuwo aona zitukuko zosiyanasiyana zomwe boma la President Lazarus Chakwera lachita ku Mangochiko.

A Chikuta anali ndi ena mwa akuluakulu achipani ku chigawo cha kummawa,pa boma komanso ku dera, kuphatikizapo m’modzi mwa amene alowa chipani cha MCP kuchokera ku DPP posachedwapa, a Imran Mtenje.

A Mtenje ati chipani cha MCP chili ndi zolinga zabwino zofuna kutukula dziko lino ndichifukwa chake sichikutekeseka ndi zomwe anthu otsutsa boma akukamba monyoza.

Iwo atinso kulowa kwa anthu ambiri m’chipanichi mchigawo  cha kummawa kukupereka umboni kuti mtsogoleri wadziko linoyu adzapambana mosavuta pa chisankho cha chaka chamawa.

M’modzi mwa amene alowa chipanichi ndi yemwe anali msungi chuma wachipani cha UDF, a Yusuf Shaibu, ndipo ati alowa chipani cha MCP chifukwa bomali likuchita zazikulu kumbali ya chitukuko.

 

Olemba: Mirriam Kaliza

Related posts

Ministry of Water warns of potential floods in Southern Region

Romeo Umali

Salima Sugar supplies product to Blantyre retailers

Blessings Kanache

Blue Eagles yayamba moyo wa ligi ya Chipiku ndichipambano

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.