Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Anayi awamanga ataba zipangizo za galimoto

Apolisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre amanga anthu anayi powaganizira kuti anathyola sitolo ndikuba zipangizo za galimoto, kuphatikizapo mabatire.

Wachiwiri kwa ofalitsankhani zapolisi ku Limbe, Chibisa Mlimbika, wati anayiwo anafika pamalo pomwe pali ofesi za kampani ya zomangamanga ya Dika Construction House ndipo anamanga mlonda asanathyole ndikuba zipangizozo.

Anthu anayiwo ndi Saidi Mambo wazaka 32, Victor Chamasowa wazaka 28, Patrick Chingwalu wazaka 25 ndi Andrew Juma wazaka 26.

Kafukufuku wa apolisi waonetsa kuti mbavazo ndi zomwenso zinakaba

zipangizo za galimoto zandalama pafupifupi K2 million kunyumba ina ku Kanjedza mumzinda womwewo wa Blantyre.

Related posts

BIRTH CERTIFICATION TO ACCELERATE DEVELOPMENT

MBC Online

MALAWI OLYMPIC COMMITTEE USHERS IN NEW OFFICE BEARERS

Rabson Kondowe

Lifa, Simwaka qualify for Cameroon’s African Senior Athletics Championship

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.