Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Anayi awamanga ataba zipangizo za galimoto

Apolisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre amanga anthu anayi powaganizira kuti anathyola sitolo ndikuba zipangizo za galimoto, kuphatikizapo mabatire.

Wachiwiri kwa ofalitsankhani zapolisi ku Limbe, Chibisa Mlimbika, wati anayiwo anafika pamalo pomwe pali ofesi za kampani ya zomangamanga ya Dika Construction House ndipo anamanga mlonda asanathyole ndikuba zipangizozo.

Anthu anayiwo ndi Saidi Mambo wazaka 32, Victor Chamasowa wazaka 28, Patrick Chingwalu wazaka 25 ndi Andrew Juma wazaka 26.

Kafukufuku wa apolisi waonetsa kuti mbavazo ndi zomwenso zinakaba

zipangizo za galimoto zandalama pafupifupi K2 million kunyumba ina ku Kanjedza mumzinda womwewo wa Blantyre.

Related posts

Lands Ministry asked to fast track construction of houses for people with albinism

Romeo Umali

Kanengo Police takes crime fight to the pulpit

Yamikani Simtowe

KATSONGA WOOS INDIAN INVESTORS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.