Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Amayi atenge mbali pa ndale — MHRC

Bungwe la Malawi Human Rights Commission (MHRC) lapempha nthambi zosiyanasiyana kuti zithandize amayi ndi kuwalimbikitsa kuti akwanitse kutenga nawo mbali pandale.

M’modzi wa akuluakulu ku MHRC, a Deborah Tambulasi Banda, ndi amene amayankhula izi pamkumano omwe anakonza ku Lilongwe ndi nthambi zosiyanasiyana pofuna kuwunikirana momwe angathanirane ndi mavuto omwe amayi amakumana nawo pa ndale.

“Tikufuna pakhale 50/50 maka pa udindo akuluakulu mundale kapena 60/40 chaka cha 2025 kupita kutsogolo,” anatero a Banda.

Wapampando wa komiti yoona zofalitsa uthenga ku nyumba ya malamulo, komanso phungu wa dera la kumadzulo kwa boma la Chikwawa, a Susan Dossi, anapempha amayi kuti azidzikhulupilira ndi kupewa kuponderezana komanso kudziyang’anira pansi pochita ndale.

Mkulu wa bungwe la Malawi Council of Disability Affairs (MACODA), a George Chiusiwa, anati ndi koyenera kuti aliyense adzitenga nawo gawo pa ndale kaamba kakuti ndi ufulu wa aliyense.

A Chiusiwa anatinso akukambirana ndi bungwe loyendetsa zisankho la MEC kuti awunikire malamulo ena omwe amapsinja anthu awulumali ngakhalenso amayi pandale.

 

Related posts

Illovo remains positive

Romeo Umali

Bridge construction excites constituents in Chitipa

Rabson Kondowe

CAF Women’s Champions League COSAFA on tomorrow

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.