Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Aloleni achinyamata kupereka maganizo ku DPP — Chimwendo Banda

Mtsogoleri wa zokambirana za m’nyumba ya malamulo a Richard Chimwendo Banda ati nthawi yakwana ku chipani cha Democratic Progressive (DPP) kuti apatseko mpata achinyamata popereka maganizo pa zinthu zochitika mchipanichi komanso m’dziko muno.

A Chimwendo Banda ayankhula  izi pamene amadzudzula a Joseph Mwanamvekha omwe ndi m’neneri wa zachuma ku chipani cha DPP kaamba konyazitsa dongosolo la chuma cha boma la chaka cha 2024/25.

A Mwanamvekha ati dongosololi silikupatsa chiyembekezo ati popeza ndalama zakunja zikupitilira kusowa, komanso kuti ngongole za boma zachuluka kwambiri.

Koma a Chimwendo Banda ati n’kosayenera kulankhula monyoza.

 

Olemba Margaret Mapando

Related posts

MAREP Phase 9 on course – Govt

Rabson Kondowe

Tiyeni tigwirizane pokonda dziko – Chaponda

Mayeso Chikhadzula

FCB rewards civil servants

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.