Malawi Broadcasting Corporation
Development Education Local Local News Nkhani

‘Achinyamata limbikirani’

Boma lati achinyamata akuyenera kuphunzira mozama ntchito zaluso ndi cholinga chakuti masomphenya adziko lino a 2063 akhale aphindu.

Nduna yazachinyamata, a Uchizi Mkandawire, yalankhula izi ku Zomba pamwambo opereka ma Certificate kwa achinyamata pafupifupi 1000 amene atsiriza maphunziro osiyanasiyana antchito zaluso.

“Mundondomeko ya achinyamata, boma likutsindika kwambiri kukweza miyoyo ya achinyamata pachuma choncho zomwe zikuchitikazi ndi imodzi mwa ntchito zomwe unduna wathu ukulimbikitsa,” anatero a Mkandawire.

Mmau ake, mkulu wa bungwe la Care Malawi, Pamela Kuwali, wati ntchito ya Titukulane yapereka kusintha kwakukulu pakati pa achinyamata amaboma a Mangochi ndi Zomba kumbali yodzipezera chuma.

Bashir Ali, mmodzi wa achinyamata omwe apindula ndimaphunzirowa, wati umoyo wake wasintha pachuma kaamba ka ntchito yake yosoka, pansi pa ntchito ya Titukulane.

Olemba: Simeon Shumba

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MEC shifts voter registration

Lonjezo Msodoka

Mayi wathawa atatentha manja a mwana wake

Davie Umar

WORLEC calls for equality, inclusivity for women in politics

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.