Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Nankhumwa akana kulankhula mawu omaliza potsekera msonkhano wa aphungu

Mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma ku Nyumba ya Malamulo, a Kondwani Nankhumwa, akana kulankhula mawu omaliza potsekera msonkhano wa aphunguwa, umene wakhala ukuchitika kwa sabata zisanu ndi zitatu.

Pamene Nyumba ya Malamulo ikumaliza  msonkhano wake lero, Sipikala wa Nyumbayi, a Catherine Gotani Hara, anapereka mpata kwa mkulu wa chipani cha DPP a Mary Navitcha kuti alankhule mau awo omaliza pa msonkhanowu, ndipo atamaliza, a Catherine Gotani Hara anaperekanso mpata kwa mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma mnyumbayi kuti nawo alankhulepo

Koma a Nankhumwa anakana kulankhula ponena kuti zomwe sipikalayu wachita polora a Navitcha kulankhula ndizosemphana ndi malamulo.

Related posts

Chileka Police officers inspire learners

Romeo Umali

Alimi aku Lilongwe asonkhanitsa K1.7 biliyoni yochitira ulimi

Alinafe Mlamba

Ministry of Education partners NCIC for quality, sustainable infrastructure

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.