Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

A Ken Msonda alowa chipani cha MCP

M’modzi mwa amene anali mamembala akuluakulu achipani cha DPP, a Ken Msonda, alowa chipani cha Malawi Congress (MCP).

A Msonda alandiridwa m’chipani cha MCP ku Mzuzu ndi mtsogoleri wachipanichi, Prezidenti Dr Lazarus Chakwera.

A Msonda anawapelekeza ndi mafumu akuluakulu aku Rumphi, kuphatikizapo mfumu yayikulu Chikulamayembe.

Poyankhula polandira a Msonda, Dr Chakwera adati khomo la chipani cha MCP ndi lotsekula ndipo onse amene akufuna kugwira ntchito ndi chipanichi ndi wolandiridwa.

M’mau awo, a Msonda anati MCP ndi chipani chokhacho chomwe chimatsata mfundo za dimokalase ndipo ndi okhutira ndi zitukuko zosiyanasiyana zimene zikuchitika m’dziko muno.

Ena mwa akuluakulu omwe adali nawo pamwambowo ndi a Harry Mkandawire, mkulu owona ndondomeko zachipani a Ken Zikhale Ng’oma, ndi m’modzi mwa magavanala a chipani cha MCP ku mpoto, a Kezzie Msukwa.

Related posts

Zomba Chingale legislator sent out for violating rules of the House

Romeo Umali

MCP lauds late Chaziya’s son for development projects

Rabson Kondowe

Lifa, Simwaka qualify for Cameroon’s African Senior Athletics Championship

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.