Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

A Ken Msonda alowa chipani cha MCP

M’modzi mwa amene anali mamembala akuluakulu achipani cha DPP, a Ken Msonda, alowa chipani cha Malawi Congress (MCP).

A Msonda alandiridwa m’chipani cha MCP ku Mzuzu ndi mtsogoleri wachipanichi, Prezidenti Dr Lazarus Chakwera.

A Msonda anawapelekeza ndi mafumu akuluakulu aku Rumphi, kuphatikizapo mfumu yayikulu Chikulamayembe.

Poyankhula polandira a Msonda, Dr Chakwera adati khomo la chipani cha MCP ndi lotsekula ndipo onse amene akufuna kugwira ntchito ndi chipanichi ndi wolandiridwa.

M’mau awo, a Msonda anati MCP ndi chipani chokhacho chomwe chimatsata mfundo za dimokalase ndipo ndi okhutira ndi zitukuko zosiyanasiyana zimene zikuchitika m’dziko muno.

Ena mwa akuluakulu omwe adali nawo pamwambowo ndi a Harry Mkandawire, mkulu owona ndondomeko zachipani a Ken Zikhale Ng’oma, ndi m’modzi mwa magavanala a chipani cha MCP ku mpoto, a Kezzie Msukwa.

Related posts

Mudzi wa aChewa autsekulira ku Lilongwe

MBC Online

KAMPANI ZACHITA BWINO CHAKA CHATHA— MCCCI

Romeo Umali

Girls urged to rise above stereotypes

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.