Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Okweza dala mitengo ya katundu nthawi yawo yatha — Mumba

Nduna ya za malonda a Vitumbiko Mumba yachenjeza kuti boma sililekelera kuti aMalawi avutike ndi kukwera kwa mitengo ya zinthu kaamba ka anthu ena adyera.
A Mumba, omwenso adzayime ndi mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pa 16 September pano, ayankhula izi m’boma la Mzimba pa misonkhano yoyimayima.
Iwo anati boma lili tchelu kuthana ndi wina aliyense yemwe akukwezera dala mitengo ya katundu pofuna kupweteka aMalawi.
Izi zikutsatira malipoti a kupezeka kwa sugar komanso cement zomwe anati anthu ena osakonda dziko lawo amabisira dala, zomwe boma la Dr Chakwera likuthana nazo.
Olemba: Grant Mhango

Related posts

Pasuwa akukhulupilira kuti Bullets iyambaso kuchita bwino

MBC Online

Children urge authorities to Address challenges in Dedza

Romeo Umali

Govt plans to transform Mzimba into an agricultural hub — Chakwera

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.