Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apolisi awapempha kulimbikitsa ntchito yoteteza amayi kunkhanza munthawi ya chisankho

Ogwira ntchito zofalitsankhani ku nthambi ya apolisi m’dziko muno awalimbikitsa kuti aike chidwi chachikulu pothandizira ntchito yoteteza amayi ku mchitidwe wa nkhanza mu nthawi ya chisankho.

Mkulu wa apolisi m’chigawo cha kummawa, Commissioner Barbra Mchenga Tsiga, walankhula izi ku Mangochi pamaphunziro a akuluakulu ofalitsankhani kunthambi ya polisi m’dziko muno.

Commissioner Barbra Mchenga Tsiga

Maphunzirowa, omwe akuchitika ndi thandizo lochokera ku UN Women, cholinga chake ndi kufuna kuzamitsa apolisi pa momwe angathandizire kuchepetsa nkhanza zomwe amayi komanso asungwana amakumana nazo pamene akutenga nawo mbali pachisankho.

Zina mwa nkhani zomwe zatuluka pa maphunzirowa ndizoti amayi ambiri amakumana ndi nkhanza  monga kuchitidwa chipongwe mmasamba amchezo apa internet pamene akuonetsa chidwi chotenga mbali pa nkhani zachisankho, choncho ndikofunika kuti adziwe zofunika kuchita  pamene akumana ndi nkhanza zotere.

 

Olemba: Owen Mavula

Related posts

SADC Calls for fresh elections in Madagascar

Romeo Umali

Malawi’s infrastructural development promising

Romeo Umali

Gawo lachitatu la kalembera wazisankho wayamba

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.