Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Mamembala a COMSIP alimbikitsa ukhondo m’misika

Bungwe la COMSIP Cooperative Union lalimbikitsa anthu kuti adzitsatira njira za ukhondo pofuna kuti adzikhala athanzi ndi kugwira ntchito zotukula mabanja komanso madera awo.

Mkulu woyendetsa ntchito za m’chigawo cha pakati kubungweli, a Annie Nyirenda, anena izi pamene anali nawo pa ntchito yapadera yosesa ndi kuchotsa zinyalala m’misika ya Area 49 ndi 4 ways mumzinda wa Lilongwe.

Mamembala a bungweli ndi ena anakonza mwambowu mogwirizana ndi khonsolo ya mzinda wa Lilongwe, pofuna kuonetsera maphunziro okhudza za ukhondo ndi kadyedwe kabwino omwe analandira kuchokera ku COMSIP.

Poyankhula m’malo mwa khonsolo ya mzinda wa Lilongwe, a Vitumbiko Lungu, anayamikira bungwelo kaambathe kogwirana manja ndi mamembala ake pa ntchito yolimbikitsa ukhondo m’madera mwawo.

Related posts

Jossam, Adam shine at Mt. Mulanje Porters Race

Romeo Umali

Car-Free Day this Friday

Romeo Umali

Mutharika confident that Itaye will deliver results

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.