Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Mamembala a COMSIP alimbikitsa ukhondo m’misika

Bungwe la COMSIP Cooperative Union lalimbikitsa anthu kuti adzitsatira njira za ukhondo pofuna kuti adzikhala athanzi ndi kugwira ntchito zotukula mabanja komanso madera awo.

Mkulu woyendetsa ntchito za m’chigawo cha pakati kubungweli, a Annie Nyirenda, anena izi pamene anali nawo pa ntchito yapadera yosesa ndi kuchotsa zinyalala m’misika ya Area 49 ndi 4 ways mumzinda wa Lilongwe.

Mamembala a bungweli ndi ena anakonza mwambowu mogwirizana ndi khonsolo ya mzinda wa Lilongwe, pofuna kuonetsera maphunziro okhudza za ukhondo ndi kadyedwe kabwino omwe analandira kuchokera ku COMSIP.

Poyankhula m’malo mwa khonsolo ya mzinda wa Lilongwe, a Vitumbiko Lungu, anayamikira bungwelo kaambathe kogwirana manja ndi mamembala ake pa ntchito yolimbikitsa ukhondo m’madera mwawo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Ntchito yopopa madzi mu nyanja ya Malawi ichepetsa vuto la madzi ku Dowa – Chakwera

MBC Online

Govt calls for multi-sectoral approach in scaling up clean energy

Mayeso Chikhadzula

Chakwera calls for nationwide prayers for missing plane

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.