Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mashehe adandaula chifukwa mabanja sakulimba

Mkulu wa ma Sheikh m’dziko muno, Grand Mufti Muhammad Uthman, wadandaula ndi mchitidwe othetsa mabanja m’dziko muno, ngakhalenso a chipembedzo cha chisilamu.

A Uthman anati, kudzera kubungwe la Islamic Information Bureau, akulandira madandaulo othetsa mabanja okwana 40 pa zana lililonse.

Iwo anati ambiri mwa iwo akumakhala achinyamata a zaka zakubadwa zapakati pa 20 ndi 35.

Iwo anati izi zili chomwechi kaamba kakuti achinyamata akumatsatira makhalidwe akunja komanso moyo otsanzira anzawo.

Chifukwa cha ichi, ofesi ya Grand Mufti of Malawi ndi Lilongwe City Centre Muslim Jamaat anayitanitsa msonkhano wa maphunziro okhudza za m’banja kwa mabanja achisalamu.

Related posts

Boma lipitiriza kumamvana ndi ma Bishopu a Katolika

Blessings Kanache

US to support Malawi in addressing food shortage

MBC Online

Disability inclusion concerns raised at National Tally Centre

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.