Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

UNDUNA WAZA CHUMA UKULINGALILA ZOONJEZELA NDALAMA KUBUNGWE LA NEEF

Nduna ya zachuma a Simplex Chithyola Banda ati unduna wao uonetsetsa kuti wapereka ndalama zokwanila ku bungwe la NEEF.

Poyankhula pomwe akuyendela ntchito za NEEF  m’maboma osiyanasiyana kuona momwe anthu akupindulila ndi ngongole za NEEF,  a Chithyola-Banda ati pomwe aphungu adzikumana kuyambila pa 9 February mwezi uno,  akaonetsetsa kuti  akambilane mozama nkhani yokhudza bungwe la NEEF lomwe ati ndalama zake zikupindulila madera onse komwe kuli aphungu.

M’mau ake nduna yazofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, ati boma la Prezidenti Dr Lazarus Chakwera likuchita chilichonse chotheka poonetsetsa kuti mdziko muno muli chakudya chokwanila nthawi zonse.

M’mau ake membala wa komiti yaikulu yoyendetsa ntchito za bungwe la NEEF a Jacob Mderu apempha anthu kuti apitilize kubweza ngongole ncholinga choti anthu ambili apindule mdziko muno.

Bungwe la NEEF analipatsa K75 billion  kuti lipereke ngongole koma panopa linadutsa kale kufika pa K87 billion.

Magulu kapena munthu m’modzi mdziko muno amatha kutenga ngongole kuyambila K1 million kapena kuposera pamenepo.

 

Wolemba Mayeso Chikhadzula.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Ramadhan starts on Tuesday

Romeo Umali

WFP donates Genset to improve NFRA’s operations

Olive Phiri

Twists and turns on Malawi Stock Exchange (MSE)

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.