Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Wakabaza waphula K200 million ya BetPawa

A Peter Vanasiyo, 28, achita mphumi pamene apambana K200 million pa masewero a juga otchedwa Aero amene amachititsa ndi a kampani ya BetPawa. Iwo anayikapo ndalama yokwana K200 yokha kuti achite mphumi.

A Vanasiyo ndi ochokera m’boma la Ntcheu ndipo ndi mlimi komanso amachita malonda oyendetsa Kabaza.

Poyankhula ku Blantyre pamene amalandira ndalamayi, Vanasiyo anati ndalamayi imuthandiza kuti ayambe mabizinesi osiyanasiyana kuphatikizapo bizinesi ya ulimi wa nthilira, umene anati umuthandiza kuti alembeko ntchito achinyamata a mdera lake.

Mkulu owona ntchito zamalonda ku mwera kwa Africa ku BetPawa, a Bwalya Musonda Noah, anati kampaniyi ili ndi kuthekera kolipira ndalama kwa anthu onse owina ngakhale munthu atawina ndalama zankhaninkhani.

A Noah anatsindikanso kuti anthu asamatenge juga ngati njira yopezera ndalama mwa changu koma adziyitenga ngati masewero chabe.

Olemba: Alufisha Fischer

Related posts

Ntchito yoponya voti ili mkati ku ward ya Mwasa

Romeo Umali

CHAKWERA LEADS MALAWIANS IN MOURNING JZU

MBC Online

Prezidenti Chakwera akhala nawo pa mwambo operekeza maliro

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.