Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mankhwala ophera tizilombo a chlorine samalepheretsa kubereka

Boma lati mankhwala ophera tizilombo a chroline alibe vuto lirilonse pa umoyo ngakhalenso nkhani zokhudza ubereki.

Wachiwiri kwanduna yoona za madzi ndi ukhondo a Liana Kakhobwe Chapota anena izi pamwambo opereka mankhwala a chroline ku khonsolo ya boma la Balaka.

Ndunayi yati sizoona zomwe anthu ena akhala akunena kuti madzi omwe ayikamo mankhwala opha tizilombo monga chlorine amalepheretsa kubereka.

Mmau ake wapampando wabungwe la Evidence Action lomwe lapereka thandizoli Dr Annie Phoya ati ndicholinga cha bungweli kuthandiza Boma pa ntchito yake yopereka madzi abwino ndi aukhondo kwa a Malawi ambiri makamaka am’madera akumidzi.

Thandizoli ndila ndalama zokwana K26 million.

Related posts

Timu ya Ekhaya ikusendera chifupi ndi ligi

Rabson Kondowe

Apha makwacha ndi ulimi wamakono wa mpunga

Alinafe Mlamba

A Sendeza alimbikitsa chilungamo pa ndondomeko ya Mtukula Pakhomo

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.