Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News

Apolisi apeza galimoto yobedwa

Apolisi ku Lilongwe apeza galimoto ya mtundu wa Nissan NP200 yomwe mbava zomwe sizikudziwika zinabera dotolo wina pa round about ya Mchinji mu msewu Bypass.

Ofalitsa nkhani ku Polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, ati izi zidachitika usiku wa pa 6 July pamene mwini galimotoyo amachokera ku Likuni kupita ku Area 47.

A Chigalu ati eni galimotowo anaima pambali pa msewu chifukwa galimoto yawo inatha mafuta ndipo akuba amene anatenga zikwanje anawakhapa ndi kuwabera galimoto koma sanapite nayo patali chifukwa apolisi amene amayendayenda m’deralo anafika pafupi ndipo mbalazo zidathawa.

Akuzungulirabe, apolisiwo anakumana ndi mwini galimotoyo ali magazi okhaokha uku akufuula kufuna chithandizo ndipo anamutenga ndi kumuuza kuti ayipeza.

Padakali pano, apolisiwo akuyang’anabe mbavazo zomwe zathawa ndi foni ya mtundu wa Itel ndi ndalama zokwana K7 thousand.

 

Related posts

MACRA set for property numbering in Nkhata Bay

Rabson Kondowe

Govt initiates construction of chiefs’ houses to improve welfare

Romeo Umali

60,000 illegal fishing gear destroyed in Nkhata Bay

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.