Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amumanga pomuganizira kuti wapha mkazi wake chifukwa cha nsanje

Chataika Makawa wazaka 45 ali mchitokosi cha polisi ku Mangochi pomuganizira kuti wapha mkazi wake Esimy Daudi wazaka 42, amene amamukayikira kuti anali ndi chibwenzi.

Ofalitsankhani za polisi ya Mangochi, Amina Tepani Daudi, wati Makawa amumanga mmudzi mwa Kwitunji mdera la mfumu yaikulu Katuli dzulo pomuganizira kuti wapha mkazi wakeyo pomubaya ndi chikwanje kumsana.

Daudi wati mukafukufuku wawo, apolisi apeza kuti banjali linali lapendapenda chifukwa mamunayu amamulonda kwambiri mkaziyo pomuganizira kuti amayenda njila zamseli.

Makawa akaonekera ku khothi kukayankha mlandu wakupha.

 

Related posts

Mera lifts ban on use of jerry cans

Romeo Umali

Govt reviews labour laws to align with global conventions

Rabson Kondowe

Chakwera applauds Malawi U19 Women’s Cricket team victory

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.