Malawi Broadcasting Corporation
International Nkhani

Chipani cha ANC chikutsogola ku South Africa

Bungwe loyendetsa chisankho mdziko la South Africa mawa lamulungu lilengeza zotsatira zonse zotsimikizika zachisankho pomwe latsala pang’ono kumalizitsa ntchito yowerengera mavoti.

Pakadali pano, chipani cholamula cha African National Congress (ANC) chikutsogola ndi mavoti oposa 41 pa 100 aliwonse omwe awerengedwa, motsatana ndi Democratic Alliance (DA) ndi 21% pomwe cha mtsogoleri wakale a Jacob Zuma, uMkhonto weSizwe (MK) ndichachitatu ndi 13% ndipo Economic Freedom Fighters (EFF) chotsogoleredwa Julius Malema ndi chachinayi ndi 9%.

Malipoti akusonyeza kuti ngati chipani cholamula cha ANC chikanike kupeza 50% ya mavoti, chikuyenera kuchita mgwirizano ndi zipani zina kuti chithe kusankha mtsogoleri wadziko, malinga ndi malamulo.

Malamulo adzikolo amati chipani chomwe chadutsa theka la aphungu anyumba yamalamulo pamavoti ndicho chimakhala ndi mphamvu yosankha mtsogoleri wadziko.

Related posts

Health Experts Gather for AHAIC 2025: Call for urgent action on Africa’s health challenges

McDonald Chiwayula

Malawi aligns with global ethical AI standards

McDonald Chiwayula

Sitima ina yonyamula mafuta iyamba kuyenda sabata ya mawa

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.