Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Nankhumwa akana kulankhula mawu omaliza potsekera msonkhano wa aphungu

Mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma ku Nyumba ya Malamulo, a Kondwani Nankhumwa, akana kulankhula mawu omaliza potsekera msonkhano wa aphunguwa, umene wakhala ukuchitika kwa sabata zisanu ndi zitatu.

Pamene Nyumba ya Malamulo ikumaliza  msonkhano wake lero, Sipikala wa Nyumbayi, a Catherine Gotani Hara, anapereka mpata kwa mkulu wa chipani cha DPP a Mary Navitcha kuti alankhule mau awo omaliza pa msonkhanowu, ndipo atamaliza, a Catherine Gotani Hara anaperekanso mpata kwa mtsogoleri wa aphungu otsutsa boma mnyumbayi kuti nawo alankhulepo

Koma a Nankhumwa anakana kulankhula ponena kuti zomwe sipikalayu wachita polora a Navitcha kulankhula ndizosemphana ndi malamulo.

Related posts

All set for 2024 National Youth Summit – NYCOM

Romeo Umali

Dr Chakwera adzudzula anthu opondereza pa ntchito ya mtukula pakhomo

Romeo Umali

Osamatchula anthu achi alubino maina onyazitsa- YONECO

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.