Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

“Ntchito zomangamanga zidzikhala zapamwamba”

Prezidenti wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, wati ndikofunika kuti makontalakitala adzigwira ntchito zapamwamba ndi zolimba.

Pa chifukwachi, Dr Chakwera walamula mlembi mu ofesi ya Prezidenti ndi nduna zake kuti aonetsetse kuti akulondoloza za nkhaniyi.

Mwazina, Dr Chakwera wati ndi wokondwa kuona kuti koleji za
aphunzitsi za Chikwawa, Rumphi komanso Mchinji TTC azimanga mwapamwamba.

Prezidenti Chakwera walankhula zimenezi pamene amatsekulira makoleji a aphunzitsi atatuwa pamwambo omwe unachitikira ku Rumphi mchigawo chakumpoto.

Mtsogoleri wa dziko linoyu ali m’chigawo chakumpoto kuyendera zitukuko zosiyanasiyana komwe watsimikiza kuti boma lake limalizitsa komanso kuyamba zitukuko zomwe anati ndi zokomera a Malawi.

Related posts

All set for official launch of Malawi School of Government

McDonald Chiwayula

Silver, CIVO cruise to Goshen Championship finals

MBC Online

National quiz contest impacts positively on Malawian learners

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.