Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mukatengera chipani njala ikusautsani, watero Kalitendere

Phungu wanyumba ya malamulo wa dera la kumpoto chakummawa kwa boma la Machinga, Ajilu Kalitendere, walangiza anthu a m’dera lake kuti alandire ufa umene boma likugawa kutsatira njala imene yagwa m’dziko muno.

A Kalitendere amayankhula ku Nainunje kwa mfumu yaikulu Kapoloma ku Machinga kumene bungwe loona za ngozi zogwa mwadzidzidzi la DoDMA lagawa matumba a ufa okwana 1,254 kwa omwe akhudzidwa ndi njala.

Iye anauza anthuwo kuti akatengera zakuti MCP ndiyomwe ikugawa ufawo pomwe iwo ndi achipani china, afa ndi njala.

Wolemba: Davie Umar

Related posts

265 Energy yamema kampani kuti zitsegule malo ogulitsa gasi

Mayeso Chikhadzula

Alimi ku Mtengowanthenga ayamikira boma pa mitengo ya fodya

Rabson Kondowe

Asiya zolemba, akufuna ku nyumba ya malamulo

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.