Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Zonse zili mchimake, yatero PP

Nthumwi 1,100 zochekera mzigawo zonse za dziko lino za chipani cha People’s zikuyembekeza kusankha atsogoleri atsopano a chipanichi pa msonkhano waukulu wa chipanichi, umene uyambe masana ano munzinda wa Lilongwe.

Padakali pano, nthumwi zikulowa mchipinda momwe muchitikire msonkhano umenewu.

Wapampando wa komiti yomwe yakonza msokhanowu, a Peter Kamange, wati maina a omwe apikisane pa maudindo osiyanasiyana awatulutsa masana ano.

“Tikutsirizitsa ntchito younika maina a omwe apikisane. Anthu angapo apereka zikalata zoti apikisane pa udindo wa mtsogoleri wa People’s kotero tikatsiriza kuunika zipepala zomwe anthu apereka, titulutsa mndandanda wonse kuti anthu onse adziwe,” atero a Kamange.

Iwo ati zonse zili mchimake, ndipo akuyembekezera kuti msonkhanowu, umene uthe mawa loweruka, uyenda bwino.

Mutu wa msonkhanowu ndi ‘Restoring the Hope: Building a Brighter Future Together’.

 

Related posts

CHAKWERA TO MEET FORMER HEADS OF STATE OVER CYCLONE FREDDY

McDonald Chiwayula

Nine Malawians to study in Ireland under Irish Aid

MBC Online

STANDARD BANK, PRESS TRUST EXTEND SECONDARY SCHOOL SCHOLARSHIPS

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.