Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiyeni tithandize anthu athu aluso

Yemwe anali mlendo olemekezeka pa mwambo owonetsa kanema wa Justice ku Lilongwe a Dalitso Kabambe wapempha a Malawi kuti aziikapo chidwi potukula aluso a mdziko muno.

A Kabambe anena izi pomwe ati mdziko muno muli aluso osiyanasiyana omwe mbali yawo akuyesetsa koma akufunikira thandizo.

“Mdziko muno muli luso ndipo kanemayi ndi umboni oti a Malawi tikukula pankhani zaluso. Zatsala kwa ife tsopano a Malawi kuti tiwapatse zoyenera alusowa kuti apitilize kutisangalatsa,” anatero a Kabambe.

M’mawu ake mkulu wa kampani ya Magic Promotions, Brazio Mathias, yemwe walemba ndikujambula kanemayi wati ndiokondwa poti pang’onopang’ono a Malawi akuvomereza kuti mdziko muno muli luso.

Iye watinso anthu okhala m’mizinda ina asadandaule poti akhala akulowera komweko kukaonetsanso kanemayi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHAKWERA HOSTS JUDGES TO DINNER

MBC Online

Chakwera graces World Creativity & Innovation Day

Eunice Ndhlovu

Pray for Malawi, says President Chakwera

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.