Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiyeni tithandize anthu athu aluso

Yemwe anali mlendo olemekezeka pa mwambo owonetsa kanema wa Justice ku Lilongwe a Dalitso Kabambe wapempha a Malawi kuti aziikapo chidwi potukula aluso a mdziko muno.

A Kabambe anena izi pomwe ati mdziko muno muli aluso osiyanasiyana omwe mbali yawo akuyesetsa koma akufunikira thandizo.

“Mdziko muno muli luso ndipo kanemayi ndi umboni oti a Malawi tikukula pankhani zaluso. Zatsala kwa ife tsopano a Malawi kuti tiwapatse zoyenera alusowa kuti apitilize kutisangalatsa,” anatero a Kabambe.

M’mawu ake mkulu wa kampani ya Magic Promotions, Brazio Mathias, yemwe walemba ndikujambula kanemayi wati ndiokondwa poti pang’onopang’ono a Malawi akuvomereza kuti mdziko muno muli luso.

Iye watinso anthu okhala m’mizinda ina asadandaule poti akhala akulowera komweko kukaonetsanso kanemayi.

Related posts

ZOMBA POLICE IMPOUNDS 18 MOTORCYCLES

Romeo Umali

Standard Bank pledges development support

Romeo Umali

First Lady inaugurates solar-powered water project

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.