Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

T/A Amidu alowa mmanda

Malemu Mfumu Yaikulu Amidu awayika mmanda lero ku likulu kwa ufumu wawo ku Nangulungutiche ku Balaka.

Mfumuyi dzina lawo lenileni linali Amina Gayesi ndipo anamwalira ali ndi zaka 56 Loweruka lapitali pa chipatala chachikulu cha Zomba atadwala nthenda ya khansa.

Pamwambowo, mlembi wamkulu ku unduna wazamaboma ang’ono, Elizabeth Chindebvu, anati unduna wawo ndiokhudzidwa ndi imfayi chifukwa mtsogoleri akachoka pamalo,chitukuko chimasokonekera.

Iwo anapempha banja lofedwa kuti lisunge bata ndi mtendere mpaka atasankha mlowammalo amene aliyense adzakhutire naye.

Wachiwiri kwa wapampando wa khonsolo ya Balaka, a Dickson Wasili, anati iwo ndiodandaula potaya mfumu yokhayo yachizimayi imene inatsala m’bomalo.

Malemu T/A Amidu asiya ana anayi.

 

Olemba: Mirriam Kaliza

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHIEFS CHALLENGED TO RECLAIM LEADERSHIP IN ECOSYSTEM RESTORATION

MBC Online

Religious leaders happy with Dr Chakwera’s development initiatives

MBC Online

Empower women, girls with disabilities — FEDOMA

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.