Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Palibe chiopsezo chilichonse’

Akuluakulu a malo ogona alendo a Mount Soche munzinda wa Blantyre ati akwanitsa kuzimitsa moto umene unabuka pamalowo.

Malinga ndi mmodzi mwa akuluakuluwo, motowo unabuka ku malo komwe amatayako zinyalala.

Iwo ati motowo sunakhudze malo eni-eni ogona alendo.

Pakadali pano, akuluakuluwo apempha alendo komanso ogwira ntchito amene anathawa pamalopo kuti abwelere, ponena kuti palibe chiwopsezo chilichonse.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Achinyamata limbikirani’

MBC Online

MUST ichititsa chionetsero cha chikhalidwe

Arthur Chokhotho

Dr Usi akhazikitsa nawo Malawi Church and Community Transformation Movement

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.