Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Palibe chiopsezo chilichonse’

Akuluakulu a malo ogona alendo a Mount Soche munzinda wa Blantyre ati akwanitsa kuzimitsa moto umene unabuka pamalowo.

Malinga ndi mmodzi mwa akuluakuluwo, motowo unabuka ku malo komwe amatayako zinyalala.

Iwo ati motowo sunakhudze malo eni-eni ogona alendo.

Pakadali pano, akuluakuluwo apempha alendo komanso ogwira ntchito amene anathawa pamalopo kuti abwelere, ponena kuti palibe chiwopsezo chilichonse.

 

Related posts

Pulezidenti wakale wa FAMA wafunira zabwino Mayi Kingston

Romeo Umali

Tambala Super Cup ayikhazikitsa

Romeo Umali

Dr Chakwera apereka ulemu omaliza kwa malemu Dr Chilima ku Nyumba ya Malamulo

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.