Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Palibe chiopsezo chilichonse’

Akuluakulu a malo ogona alendo a Mount Soche munzinda wa Blantyre ati akwanitsa kuzimitsa moto umene unabuka pamalowo.

Malinga ndi mmodzi mwa akuluakuluwo, motowo unabuka ku malo komwe amatayako zinyalala.

Iwo ati motowo sunakhudze malo eni-eni ogona alendo.

Pakadali pano, akuluakuluwo apempha alendo komanso ogwira ntchito amene anathawa pamalopo kuti abwelere, ponena kuti palibe chiwopsezo chilichonse.

 

Related posts

President Chakwera ayendera ntchito zachitukuko ku Mangochi

Romeo Umali

Aloza chala maboma akale posalabadira nsewu wa Karonga-Chiweta

Romeo Umali

Wakabaza waphula K200 million ya BetPawa

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.