Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Sitalaka ya madalaivala yaonongetsa mkaka wa K120 million

Alimi a ng’ombe za mkaka m’chigawo cha ku m’mwera apempha madalaivala agalimoto zikuluzikulu kuti asiye kunyanyala ntchito chifukwa akutaya mkaka wambiri.

Dzulo lokha, alimiwa ati ataya malita 240 sauzande omwe ndi wa ndalama zokwana pafupifupi K120 million kaamba kakuti galimoto zikuluzikulu zonyamula mkaka sizikuyenda.

Poyankhula pa msonkhano wa olembankhani kwa Bvumbwe m’boma la Thyolo, wapampando wa Farmers Milk Producers Association (FAMPA), a Foster Mulumbe, anati akufuna zokambirana zipitilire pakati pa magulu onse okhudzidwa pa nkhani yonyanyala ntchitoyi uku ntchito zina zonse zikuyenda.

A Mulumbe anati izi zili chomwechi chifukwa alimi awo akusowa mtengo ogwira.

Lachitatu, madalaivalawa amanyanyala ntchito yawo pofuna mabwana awo kuti awakwezere malipilo awo apa mwezi, mwa zina.

Olemba: Geoffrey Chinawa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tiwapatsa mwayi wa ngongole kuti apeze mpamba — TEVETA

Aisha Amidu

Amangidwa kaamba koganiziridwa kuti adagwilirira mwana

Charles Pensulo

MCP ipitiriza kukwaniritsa malonjezo — Kabwila

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.