Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mafumu asayina mgwirizano wa chitukuko ndi kampani ya Globe Metals and Mining

Mafumu a m’maboma a Mzimba ndi Kasungu asayinira mgwirizano ndi akuluakulu a kampani ya Globe Metals and Mining womwe uthandize kuti anthu a mmadera ozungulira mgodiwu apindule pa chitukuko cha mgodi wa Kanyika, omwe uli m’dera la Inkosi Mabilawo m’boma la Mzimba.

Mlendo wolemekezeka pa mwambowu, Inkosi ya Makhosi Mmbelwa yachisanu, inayamikira magulu awiriwa posayinira mgwirizanowu ndipo inapempha anthu mderali kuti agwirizane kuti derali lipindule ndi ntchitoyi.

Boma la Malawi linasayinira kale mgwirizano ndi Kampani ya Globe Metals and Mining chaka chatha.

Kusayinira kwa mgwirizanowu pakati pa mafumu ndi kampaniyi ndi imodzi mwa ndondomeko zomwe zili mmalamulo atsopano a zamigodi, Mines and Minerals Act 2023.

 

Related posts

NEEF yati ipitilira kuthandiza anthu

Romeo Umali

Apostle Kawinga agawa chimanga, mabaibulo Ku Mchinji

Yamikani Simtowe

John Okafor (Mr Ibu) wamwalira

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.