Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

OXFAM yaika padera K650m yothandizira amayi pandale

Bungwe la Oxfam lati lalandira K650 million yoti igwire ntchito yothandizira ndondomeko yolimbikitsa amayi kutenga nawo gawo pandale.

Mkulu wa bungweli a Lingalireni Mihowa, wanena izi ku Lilongwe pomwe amasainirana ndi unduna owona zoti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo.

A Mihowa ati kudzera mundondomeko ngati yomweyi mu chaka cha 2019 kwanthawi yoyamba anakwanitsa kupezetsa aphungu anayi m’boma la Mangochi ndipo ati ulendo uno chidwi aika m’maboma awiri, Nkhotakota ndi Mangochi.

“Tili ndi umboni kuti ntchitoyi ili ndi phindu. Taonjezerapo boma la Nkhotakota kaamba koti pakadali pano kulibeko phungu wachizimayi,” anatero a Mihowa.

M’mawu ake nduna yoona zakuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo a Jean Sendeza ati ndiokondwa kaamba koti zomwe likupanga bungweli zikugwirizana ndi masomphenya a mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera otukula amayi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bangwe yapha Bullets

MBC Online

Amugwira chifukwa chotentha manja a mwana wake

MBC Online

Alimi ndi okhutira ndi kampani zogula fodya

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.