Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

“Ndabwela kudzagwira ntchito” — Uladi Mussa

Yemwe anali wachiwiri kwa prezidenti wachipani cha Democratic Progressive Party (DPP), a Uladi Mussa, wati agwira ntchito limodzi ndi atsogoleli achipani cha MCP pofuna kuonetsetsa kuti chipanichi chipitilire kukhala champhamvu.

A Mussa amayankhula ku Dedza pabwalo la Phillip Holseman kumene mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera amachititsa msonkhano wa chitukuko.

Mwa zina a Mussa ati ma area omwe adawakhazikitsa okwana 188 tsopano awasandutsa kukhala a chipani cha MCP.

Iwo adalowa m’chipani cha MCP masiku apitawa kuchoka kuchipani cha DPP ati poona mfundo zabwino zomwe mtsogoleri wa dziko lino akutsatila potsogolela dziko lino.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Parliamentarians urged to push for increased health allocation for women, children

Olive Phiri

NBM donates K2 million to support Business Journalists’ AGM

Arthur Chokhotho

Mafumu asayina mgwirizano wa chitukuko ndi kampani ya Globe Metals and Mining

Chimwemwe Milulu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.