Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Osamatchula anthu achi alubino maina onyazitsa- YONECO

Bungwe lolimbikitsa ufulu wa anthu a chialubino la Standing Voice lati ndi zokhumudwitsa kuti anthu ambiri akupitilira kutchula anthuwa maina onyazitsa, zomwe ati ndi kuphwanya ufulu wawo.

Mkulu wa bungweli, a Boniface Massa amayankhula izi pamene bungweli pamodzi ndi mabungwe a YONECO ndi Beyond Suncare amaphunzitsa anthu za ufulu wa anthu a chi alubino pa msika wa Govala m’boma la Zomba.

A Massa ati a Malawi akuyenera kudziwa kuti kutchula anthu achialubino maina onyazitsa zimakhumudwitsa anthuwa ndipo izi ndi nkhanza zomwe zimawabwezera m’mbuyo, zomwenso ndi kulakwila malamulo.

“Enanso akuphwanya fuku wa anthuwa ochita ukwati ndi zina zambiri. Ichi ndi chifukwa tikuyendayenda kuwadziwitsa anthu za kuyipa kosala anthu a chialubino,” atero a Massa.

Mkulu wa bungwe la YONECO, a Mac Bain Mkandawire ati kugwiritsa ntchito zisudzo ndi magule zikuthandiza kwambiri kuti anthu adzifika ndi kumva uthenga ofunikawo.

Malinga ndi mkulu oyendetsa ntchito zoti apolisi adzigwira ntchito limodzi ndi anthu m’boma la Zomba, a Naison Chibondo, mchitidwe wa nkhanza kwa anthu a chialubino ukuchepa m’bomalo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chikho cha K10 million achikhazikitsa m’boma la Chikwawa

MBC Online

Apolisi agwira ozembetsa makala komanso kulanda galimoto ku Blantyre

Mayeso Chikhadzula

Malawi Fertilizer Company itha kupanga fertilizer okwana 150, 000 tons

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.