Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Okweza dala mitengo ya katundu nthawi yawo yatha — Mumba

Nduna ya za malonda a Vitumbiko Mumba yachenjeza kuti boma sililekelera kuti aMalawi avutike ndi kukwera kwa mitengo ya zinthu kaamba ka anthu ena adyera.
A Mumba, omwenso adzayime ndi mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pa 16 September pano, ayankhula izi m’boma la Mzimba pa misonkhano yoyimayima.
Iwo anati boma lili tchelu kuthana ndi wina aliyense yemwe akukwezera dala mitengo ya katundu pofuna kupweteka aMalawi.
Izi zikutsatira malipoti a kupezeka kwa sugar komanso cement zomwe anati anthu ena osakonda dziko lawo amabisira dala, zomwe boma la Dr Chakwera likuthana nazo.
Olemba: Grant Mhango
Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MACRA yaika padera K6 billion yotukula ntchito za luso lamakono

Beatrice Mwape

Kasungu Municipality elects new mayor

MBC Online

NGOKWE COMMUNITY TAKES LEGISLATOR TO TASK

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.