Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani Religion

Abusa awapempha kukhala zitsanzo pantchito yawo

Mlembi wamkuru wa mpingo wa Zambezi Evangelical a Robert Yanduya ati ndipofunika kuti abusa mu mpingowu akhale zitsanzo zabwino pautumiki wawo ati poti anthu masiku ano amalemekeza ntchito zamunthu kuposa udindo.

A Yandura anena izi pomwe mpingowu umakhazikitsa m’busa wa mpingo wa Kawale Zambezi evangelical ku Lilongwe a Duncan Ng’oma omwe posachedwapa anasankhidwanso kukhara wachiwiri kwa wapampando wa sinodi ya mpingowu.

A Ng’oma ati kubwera kwawo pampingowu kukhala kwachabe ngati satumikira bwino kudzera muntchito zawo.

Iwo alonjeza kugwira ntchito ndi nthambi zonse zapampingowu ndicholinga chofuna kupititsa patsogolo ntchito ya Mulungu. A Ng’oma atinso akudziwa kuti anthu ali ndi chiyembekezo chochuluka koma ati achilimika pa Ambuye kuti akwanilitse maitanidwe awo pampingowu.

 

Related posts

Dr Usi attends Thanksgiving, farewell mass

Romeo Umali

Talandira K6 miliyoni koma siyokwanira — Silver Strikers

Romeo Umali

NEEF iyamba kugawa ngongole za ulimi wamthilira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.