Mmodzi mwa anthu amene amayankhulapo pa nkhani zosiyanasiyana, maka zolimbikitsa ulamuliro wabwino, a Undule Mwakasungula, ati dongosolo la zachuma lomwe alipereka mnyumba ya malamulo lachisanu a nduna a zachuma, a Simplex Chithyola Banda, ndi mbambande.
Iwo ati ndondomekoyi ithandiza kutukula miyoyo ya anthu m’dziko muno.
A Mwakasungula anena izi a Banda atapereka ndondomeko yazachuma yachaka chino kufikira chaka chamawa ya ndalama zokwana K5.9 trillion.
A Mwakasungula ati dongosolo latsopanoli laonetseratu kuti boma laika chidwi pantchito yotukula miyoyo ya a Malawi.