Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Mwakasungula ati bajeti ili bwino zedi

Mmodzi mwa anthu amene amayankhulapo pa nkhani zosiyanasiyana, maka zolimbikitsa ulamuliro wabwino, a Undule Mwakasungula, ati dongosolo la zachuma lomwe alipereka mnyumba ya malamulo lachisanu a nduna a zachuma, a Simplex Chithyola Banda, ndi mbambande.

Iwo ati ndondomekoyi ithandiza kutukula miyoyo ya anthu m’dziko muno.

A Mwakasungula anena izi a Banda atapereka ndondomeko yazachuma yachaka chino kufikira chaka chamawa ya ndalama zokwana K5.9 trillion.

A Mwakasungula ati dongosolo latsopanoli laonetseratu kuti boma laika chidwi pantchito yotukula miyoyo ya a Malawi.

Related posts

Bus ya Bullets yachotsedwa ku khothi

Blessings Kanache

Anthu 1.4 million alowa nkaundula wa zipangizo zaulimi zotsika mtengo

Rabson Kondowe

Tiyeni tiphunzirepo pa moyo wa Dr. Chilima – St Patrick’s Parish

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.